Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amugwira chifukwa chotentha manja a mwana wake

Apolisi kwa Makawa m’boma la Mangochi agwira Gladys Lingoni azaka 41 powaganizira kuti anatentha manja a mwana wawo wamwamuna wazaka zisanu ndi chimodzi chifukwa chokuti anadya ndiwo za soya.

Ofalitsa nkhani za Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi ati mayiwa adathawa pa 1 mwezi omwe uno m’mudzi mwa Matuwi 2 kwa Mfumu yaikulu Mponda, komwe adasiya mwanayu ali mu ululu osasimbika.

“Mayiwa tikuwaganizira kuti anatentha mwana wawo manja onse awiri ndimajumbo chifukwa chakuti anadya ndiwo za soya zomwe anakonza kuti adyere nsima madzulo atsikulo,” anatero Daudi.

Mwanayo adalandira thandizo lamankhwala kuchipatala chaboma cha Mangochi koma anamutumiza kuchipatala cha Queen Elizabeth ku Blantyre kukalandira thandizo lapadera. Iwowa akayankha mulandu ofuna kuvulaza munthu.

 

Olemba Davie Umar

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Pray for Malawi, says President Chakwera

Romeo Umali

JICA impressed with KIA operations

Lonjezo Msodoka

PARTNERSHIPS KEY TO ENHANCED WATER SUPPLY – GOVT

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.