Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Amabera anthu powanamiza kuti amachulukitsa ndalama

Apolisi ku Zomba amanga sing’anga wa ku Mozambique, Asima Abdul, pomuganizira kuti waba ndalama za mayi wina pomunamiza kuti ali ndi mankhwala ochulukitsa ndalama.

Ofalitsankhani wapolisi ku Zomba, Patricia Sipiliano, wati Abdul, yemwe ali ndi zaka 31, anauza mayi Linda Mfupika kuti amupatse ndalama zokwana K125,000 kuti azichulukitse mukanthawi kochepa.

Koma mayiyo anadabwa kuti nthawi ikudutsa ndipo ndalamazo sizikuchuluka.

Atamufunsa, sing’anga wachinyengoyo anauza mayiyo kuti azimu akana ndalamazo chifukwa zachepa ndipo awonjezere.

Apa mayi Mfupika anazindikira kuti munthuyo ndi wachinyengo ndipo anakanena ku polisi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Defence wants Mary Bushiri discharged from extradition case

Olive Phiri

Pempho layankhidwa — Aphunzitsi okhudzidwa

Paul Mlowoka

Chakwera visits Mzuzu Flea Market

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.