Malawi Broadcasting Corporation
Uncategorized

Aliyense apindula ndi ntchito zachitukuko cha boma- Chimwendo Banda

Nduna ya maboma ang’ono, Richard Chimwendo Banda, yati boma lipitiriza kuonetsetsa kuti miyoyo ya anthu ammadera akumidzi ikusintha kudzera mu ntchito zachitukuko.

Ndunayi yanena izi ku Makanjira m’boma la Mangochi pamene imayendera zina mwa ntchito zachitukuko zomwe boma likugwira kudzera ku khonsolo ya bomali.

Mwazina, ndunayi pamodzi ndi nduna ya zaumoyo, Khumbize Kandodo Chiponda, yayendera ntchito yomanga bridge ya Lukoloma yandalama zopyola K3 billion, yomwe akuigwira pofuna kuchepetsa mavuto amayendedwe pakati pa anthu oyenda msewu wa Mangochi-Makanjira.

Ndunazi zayenderanso ntchito yomanga chipatala cha Makanjira, yomwe I kuyembekezeka kufika kumapeto mwezi wa January chaka chamawa.

Olemba: Owen Mavula

Related posts

Voters urged to verify names ahead of By-Elections

Steve Dakalira

LOWER SHIRE FACES FLOODS THREAT

MBC Online

COURT ADJOURNS NOCMA FUEL CONTRACT CASE

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.