Malawi Broadcasting Corporation
Local

ALIMI A MTEDZA APINDULA

Kampani yolimbikitsa ulimi ya Pyxus International yati ifikila alimi ochuluka ndi luso lamakono lomwe lithandize kuti mtedza olimidwa mdziko muno ukhale ovomerezeka ku misika ya pa dziko lonse.

Mkulu wa kampaniyi a Peiter Sikkel anena izi atakumana ndi mtsogoleri wa dziko la Malawi, Dr Lazarus Chakwera, pambali pa mnsonkhano wa bungwe la United Nations omwe ukuchitikira mu mzinda wa New York, m’dziko la America.

Iwo ati kampani yawo yakonzeka kuthandiza alimiwa ndi mbewu ya mtedza komanso kuwapezera misika yakunja.

Kampani ya Pyxus Agriculture Limited Malawi, ikugwila kale ntchitoyi ndi ndalama zochokera ku USAID komwe alimi ayamba kale kupindula.

 

#mbcmw
#mbcnewslive
#mbconlineservices

Related posts

Nsanje Council for adoption of modern farming techniques

Rabson Kondowe

NBS takes executive and private banking to Zomba

Rabson Kondowe

MARANATHA STUDENTS REACH OUT TO CYCLONE FREDDY SURVIVORS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.