Malawi Broadcasting Corporation
Africa Culture Local News Nkhani

ADABWA NDI KUDABWA KWA MAFUMU

Bungwe la Mulakho wa a Lhomwe lati ndi lodabwa ndi mafumu ena omwe sakumvetsa zakusankha kwa mfumu yatsopano ya a Lhomwe Paramount Chief Kaduya.

Wapampando wa bungwe-li, a Muchanakwaye Mpuluka alankhula izi pamene mafumu ena atatu anauza olembankhani lachisanu lapitali kuti sakugwirizana ndi m’mene asankhila mfumu yatsopanoyi.

Mwambo wa Mlakho wa aLhomwe

Koma a Mpuluka ati anthu-wa anali nawo pazokambirana ndipo onse anagwirizana zosankha a Kaduya ngati mfumu yawo.

Iwo adaonjezeranso kumema ma membala a bungwe lawo kuti apewe kumvera anthu andale amene akufuna kuwagawanitsa.

Lachitatu lapitali, mtsogoleli wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera adavomereza dzina la a Kaduya kuti ikhale mfumu.

Kusankha-ku kunali kukhazikitsa mfumu patadutsa zaka zoposa zisanu, potsatira imfa ya mfumu yaikulu Ngolongoliwa.

Olemba: Blessings Kanache

Related posts

FAM selects 27 footballers for Luwinga Inclusive Academy

Romeo Umali

A CHAPONDA ALI PA MSONKHANO WINA NGATI WACHIWIRI KWA MTSOGOLERI WA DPP

MBC Online

Prophet, accomplice nabbed for fraud

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.