Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Boma likuyika maziko a chitukuko — Dr Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati boma likuyika maziko okhazikika oti apindulire dziko lino kuyambira panopa mpakana mibadwo yamtsogolo.

Dr Chakwera amayankhula izi pa Kabwinja, kuzambwe kwa boma la Dowa, pamene amalankhula ndi a Malawi.

Iwo anati ngakhale dziko lino lakumana ndi ziphinjo zambiri, makamaka ngozi zogwa mwadzidzi muzaka zinayi zapitazi, zinthu zikuyenda kumbali ya ntchito zomangamanga monga misewu, nyumba za anthu ogwira ntchito ku nthambi zachitetezo ndi sukulu.

Mtsogoleriyu anati boma lionjezera chiwerengero cha opindula ku thandizo la chakudya komanso fetereza ndi mbewu zotsika mtengo kaamba kakuti limamvera zofuna za a Malawi.

Iwo anaonjezeranso kuti misewu ya kumidzi ailambula kuti alimi adzitumiza mbewu ku misika mosavuta.

Mfumu Chakhaza yaderalo inayamika boma chifukwa cha ulimi wa nthilira umene ukuchutika mderalo pa mahekitala 483, komanso chifukwa chofikitsa magetsi ndi netiweki ya lamya za mmanja.

Olemba: Isaac Jali

Related posts

MACRA to combat hacking, fraud through new campaign

Romeo Umali

Lekani kutchetcha chimanga m’minda — Boma lauza LCC

Rabson Kondowe

JB hails Chakwera for State of Disaster declaration

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.