Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Ogwira ntchito ku Premier Bet wamangidwa atachitila juga ndalama za kampani

Apolisi ku Lilongwe agwira a Rodney Kandulu a zaka 25 zakubadwa powaganizira kuti anawononga ndalama zokwana K18 million za kampani ya Premier Bet, komwe amagwira ntchito, poyichitila juga pa masewero otchedwa ‘Navigator’ mu ofesi mwawo.

Ofalitsa nkhani ku Polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu, ati a Kandulu, omwe amagwira ntchito ngati otolera ndalama ku ofesi ya Premier Bet ya ku Area 3, anapalamula mlanduwu pa 4 August 2024, lomwe linali tsiku Lamulungu.

Atatolera ndalama zomwe ofesi yawo inapanga patsikuli, iwo anayamba kuzitchovera juga n’cholinga chofuna kupeza phindu.

Koma itakwana 12 koloko masana, mabwana awo anapeza kuti ndalama ina ikusowa ndipo bambowa anawapeza kuti amachita zinthuzi pa foni yawo ndipo apolisi anathamangira kumaofesiko kudzawanjata.

Poyankha mafunso kwa apolisi, a Kandulu anavomereza kulakwa kwawo ndipo anati ndi achisoni chifukwa sangakwanitse kubweza ndalama zonsezo.

Iwo akawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa kuti akayankhe mlandu okuba pa ntchito.

A Kandulu ndi ochokera m’mudzi mwa Bismark m’dera la mfumu Kapeni m’boma la Blantyre.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Ophunzira ayenera kugwitsa ntchito bwino ndalama

Timothy Kateta

Anthu ochuluka asonkhana ku maliro a Hope Chisanu

MBC Online

Wapha munthu chifukwa cha nsanje

Charles Pensulo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.