Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Msonkhano waukulu wa CCAP Livingstonia Synod wayambika

Akuluakulu a mpingo wa CCAP mu synod ya Livingstonia akukumana ku Embangweni ku tchalichi cha Laudon m’boma la Mzimba.

Moderator wa Mpingowu M’busa Rueben Msowoya akuyembekezeka kutula pansi udindowu ndipo mmalo mwake M’busa Jairos Kamisa ndi amene atenge udindo wa Moderator watsopano.

Nthumwi zikuyenera kuchita chisankho chosankha moderator amene adzatenge udindowo mchaka cha 2026.

Pamapeto pa mkumanowu moderator mogwirizana ndi komiti yayikulu akuyembekezeka  lkusankha adindo atsopano amene agwire ntchito m’mipingo, nthambi ndi mabungwe onse a synodiyi kwa zaka ziwiri zikubwerazi.

Pamwambowu pafika akukuakulu a boma kuphatikizapo Sipikala wanyumba yamalamuro a Catherine Gotani Hara, nduna yaza ulimi a Sam Kawalex ndi alendo ena osiyanasiyana.

 

Olemba  Hassan Phiri

Related posts

IMF PROJECTS 3.3% GROWTH FOR MALAWI IN 2024, FINANCE MINISTER HAILS ECONOMIC TRANSFORMATION

McDonald Chiwayula

Nsanje DC pushes for irrigation farming

Romeo Umali

Paramount Gomani V calls on Maseko Ngoni to live peacefully with other tribes

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.