Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

TEVETA yati aliyense atha kuchita ntchito zamanja

Bungwe la Technical Entrepreneurial Vocational and Education Training Authority (TEVETA) likulingalira zolimbikitsa ndondomeko yofuna kuti maphunziro a ntchito za manja afikire anthu onse.

Wapampando wa bungweli, a Pyoka Tembo, amayankhula izi m’boma la Mulanje pamene amapereka malo ophunzirapo ntchitoyi otchedwa Ndanga, amene anawakonzanso atawonongeka ndi namondwe wa Anna ndi Gombe.

A Tembo anati achinyamata okhawo a luso ndi omwe angakwanitse kuthandidzira pa chitukuko chadziko lino.

M’modzi mwa amene watsiliza maphunziro a ulimi wa nkhumba, a Mary Maseko, anati maphunziro awo awapatsa kuthekera koti apeze phindu loyenelera mu ulimi wawo.

Pa mwambowu, TEVETA inaperekanso masitifiketi kwa anthu 125 omwe atsiriza maphunziro a ntchito zamanja monga zomangamanga, zaulimi wa nkhumba ndi luso losoka zovala.

 

Related posts

Sports is a tool to transform the youths — Inkosana Nkosi

Romeo Umali

Digital inclusion vital for achieving Malawi 2063 – MACRA

Rabson Kondowe

Champiti is CEO of Roads Authority

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.