Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Business Development Local Local News Nkhani

Alimi ndi okhutira ndi kampani zogula fodya

Alimi a fodya a m’maboma a Kasungu ndi Dowa ati ndi okhutira ndi kuchuluka kwa kampani zogula fodya pa msika omwe watsegulira lero mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

Ena mwa alimiwa ati fodya wa kontalakiti komanso auction akumugula pa mitengo ya bwino kwambiri kusiyana ndi zaka zam’mbuyomo.

Iwo ati akugulitsa fodya wawo wa kontalakiti pansi pa kampani za Nyasa Tobacco, JTI ndi Alliance One, mwa ena.

Pomwe amatsekulira msika wa fodya wa chaka chino ku Chinkhoma m’boma la Kasungu, fodya amamugula pa mtengo wa $3.01 ndipo wotsika amafika pa $2.55.

Mabelo wokwana 2, 165 ndi omwe awagulitsa koma msikawu umatha kugulitsa mabelo 7,000 patsiku.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

CHAKWERA FOR COMMERCIAL FARMING

McDonald Chiwayula

Tiyeni tithandize anthu athu aluso

Rabson Kondowe

Human Resource professionals key to development — NyaLonje

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.