Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Zaka zitatu pogulitsa makala mosatsata lamulo

Khothi la Magistrate mu mzinda wa Blantyre la lamula kuti abambo atatu akagwire ukayidi kwa zaka ziwiri komanso chaka ndi theka kaamba kopezeka olakwa pochita malonda ogulitsa makala opanda chiphaso komanso kuzembetsa zinthu za munkhalango.

Popereka chigamulo, Magistrate Godfrey Balaka anati zilango zonsezi ziyendera limodzi pofuna kuti anthu ena atengerepo phunziro ndipo mlanduwu adapalamula pa 17 April, 2024.

Nthambi za boma monga Police, ACB ndi nthambi ya zankhalango padakali pano zikugwira limodzi ntchito yothandiza kuteteza zachilengedwe.

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Govt, UNDP launch Africa Green Business and Financing Initiative Roadmap

Olive Phiri

Mia describes education as an enabler for Malawi 2063

Charles Pensulo

Let’s support MRCS’s Flag Week — Chakwera

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.