Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Zaka zitatu pogulitsa makala mosatsata lamulo

Khothi la Magistrate mu mzinda wa Blantyre la lamula kuti abambo atatu akagwire ukayidi kwa zaka ziwiri komanso chaka ndi theka kaamba kopezeka olakwa pochita malonda ogulitsa makala opanda chiphaso komanso kuzembetsa zinthu za munkhalango.

Popereka chigamulo, Magistrate Godfrey Balaka anati zilango zonsezi ziyendera limodzi pofuna kuti anthu ena atengerepo phunziro ndipo mlanduwu adapalamula pa 17 April, 2024.

Nthambi za boma monga Police, ACB ndi nthambi ya zankhalango padakali pano zikugwira limodzi ntchito yothandiza kuteteza zachilengedwe.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Mtukula pakhomo wammizinda ukhazikitsidwa lero

Blessings Kanache

CHAKWERA FOR BETTER WELFARE OF TRADITIONAL LEADERS

MBC Online

Zomba ready for e-payment system

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.