Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

Unduna wazantchito watseka mbali ina ya Makandi Tea Estate

Unduna wa zantchito, watseka mbali ina ya Makandi Tea Estate imene ili m’boma la Thyolo chifukwa chophwanya ena mwa malamulo antchito.

Mbaliyi ndi kumene kuli minda ya tiyi ndipo kumadziwika kuti ku 17 A.

Mwazina, a Mumba apeza kuti pamalopa, palibe madzi aukhondo, zimbudzi komanso ogwira ntchito ake alibe zipangizo zowatetezera pamene akugwira ntchito yawo.

Pakadali pano, ndunayi yapereka masiku asanu ndi awiri kuti kampaniyo ikhale itakonza zolakwikazo komanso alamula eni kampaniyo kuti apereke malipiro onse a ogwira ntchito kumbali yomwe ayitsekayi ngakhale kuti sakugwira ntchito.

Mmodzi mwa akuluakulu a kampaniyo, a Joe Palani, ati ayetsetsa kukonza zonse zolakwika mmasikuwo.

A Mumba akuyendera kampani za m’chigawo cha ku m’mwera potsatira madandaulo amene anthu ochuluka kuphatikizapo ogwira ntchito m’malowa akhala akupereka.

 

Related posts

Ana aphunzitsidwe njira zodzitetezera ku nkhanza zogwiliridwa

Romeo Umali

Boma, asodzi agwirana manja pofuna kuchulukitsa nsomba m’nyanja ya Malawi

Romeo Umali

Top performing teachers awarded

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.