Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Unduna waza umoyo ulitcheru pothana ndi kufala kwa matenda a kolera – Chikumbe

Unduna waza umoyo wati walandira katemera wa matenda a cholera 720,185 wa mkamwa kuchokera ku bungwe laza umoyo pa dziko la World Health Organization (WHO).

Mneneri ku unduna waza umoyo, a Adrian Chikumbe, anena zimenezi pomwe zadziwika kuti anthu ena m’maboma a Chitipa, Karonga, Balaka komanso Machinga apezeka ndi matenda wotsekula m’mimba a kolera.

A Chikumbe ati akugwira limodzi ntchito ndi ma unduna osiyanasiyana ndi mabubgwe okhudzidwa pofuna kudziwitsa anthu momwe angalimbanilane ndi matendawa.

Malinga ndi a Chikumbe, katemera amene alandira amupereka m’maboma onse omwe mwabuka matenda a kolera.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Airtel Africa expresses commitment towards improving teachers’ lives

MBC Online

KIA Police celebrates Christmas with children

MBC Online

AFREXIM BANK COMMITS TO GIVE MW $700 MN FOR ECONOMIC RECOVERY

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.