Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Tisafalitse zopanda umboni

Nduna ya zofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu ati nkulakwira malamulo kumafalitsa nkhani zomwe zilibe umboni pankhani ya kusowa kwa ndege yomwe wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Saulos Chilima anakwera.

A Kunkuyu ati nthawi ino, ndi nthawi yoti tigwirane manja ndikupemphera ngati dziko kuti omwe akusaka ndege yi athe kubooleza.

Ndunayi yati bungwe la MACRA lalumikizana ndi mabungwe ena monga la ku Zambia komanso ku Angola kuti athandizire kupeza komwe ndege yi yagwera.

Iwo ati boma molumikizana ndi maiko ena achi ta chilichonse chothekera kusaka komwe ndege yi ili.

 

Related posts

Abambo ambiri siali pa ndondomeko yama ARV — Nyirenda

Romeo Umali

Court to deliver verdict on bus depots case in September

Rabson Kondowe

‘UTM, Kabambe missed opportunity to honour SKC’s legacy’

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.