Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local Local News Nkhani

Tilime mbewu zambiri zopilira ku n’gamba — Bushiri

M’neneri Shepherd Bushiri wa mema aMalawi kuti ayambe kulima mbewu zosiyanasiyana komanso zimene zili zopilira ku ng’amba ndi cholinga chofuna kupewa njala.

A Bushiri amayankhula izi ku Masasa mu mzinda wa Mzuzu komwe iwo amagawa chimanga kwa anthu amene njala idawakhudza.

“Monga ine kumunda kwanga ndinalima chinangwa chambiri ndipo chachita bwino kwambiri,” iwo anafotokoza.

A Bushiri ali ndi chikonzero chofuna kufikira maanja okwana 1 Million ndipo ati padakali pano anthu okwana pafupi-fupi 600,000 ndi amene athandizidwa kale.

Olemba: Henry Haukeya
#MBCOnlineServices

Related posts

Farmers urged to maximise pigeon peas profits amid high global demand

Rabson Kondowe

Sant’Egidio launches book to promote child registration

Romeo Umali

MRCS yagawa K180 million m’boma la Karonga

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.