Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Tili okondwa ndi zitukuko za Dr Chakwera’

Mfumu yayikulu Nsabwe ya m’boma la Thyolo yathokoza mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera kaamba kogawa zitukuko m’madera onse mosayang’ana nkhope.

Mfumuyi yati mwazina, anthu a m’dera lake ndi okondwa ndi ndalama za mtukula pakhomo zomwe akulandira.

“Mudzitiyendera pafupipafupi ife mafumu ndi anthu adera lino tigwira ntchito ndi boma,” iwo anatero.

Iwo amayankhula pamene membala wamkulu wa chipani cha Malawi Congress, a Brown Mpinganjira, akuchititsa msonkhano pa Mathiya ku Thekerani m’bomalo.

 

Olemba : Geoffrey Chinawa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Talandira K6 miliyoni koma siyokwanira — Silver Strikers

Emmanuel Chikonso

Mashehe adandaula chifukwa mabanja sakulimba

Austin Fukula

MUBAS students aim to help fellow student

Juliana Mlungama
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.