Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Thupi la mfumu Mgulumia ya m’boma la Machinga lalowa mmanda

Unduna wa za maboma ang’ono, umodzi ndi chikhalidwe wapempha akubanja kwa malemu mfumu Mgulumia ku Machinga kuti atsate ndondomeko zonse zoyenera posankha mfumu ina yatsopano.

Mlembi wamkulu mu undunawu, Elizabeth Gomani Chindebvu alankhula izi pa mwambo oika mmanda thupi la malemu Mgulumia ku Likwenu ku likulu la mfumuyi.

“Nthawi ikafika yosankha mfumu yatsopano, kambilanani mwabata motsata chikhalidwe cha kuno komanso malamulo aboma kuti pasakhale ziwawa,” watero mlembiyu.

Malinga ndi mlembiyu, nthawi zambiri kusamvana pa za mlowammalo wa mfumu kumabwenzeletsa m’mbuyo  ntchito za  mmadera pamene mfumu ya mwalira.

Mmau ake mfumu yaikulu Chamba yomwe inaimila mafumu a  Ndodo m’bomali yati malemu mgulumia anali mfumu odzipereka  polimbikitsa umodzi  komanso ntchito za chitukuko.

Mfumu Mgulumia omwe dzina lawo lenileni ndi a Magret Askimu Mlomba amwalira dzuro loweruka ku Machinga atadwala kwa kanthawi.

A Mgulumia omwe anabadwa pa 12 october mchaka cha 1971 asiya ana anayi ndi zidzukulu ziwiri.

 

Olemba: Owen Mavula

Related posts

I am ready to serve Malawians — Mumba

Romeo Umali

How Wanderers became mighty in 2025

Romeo Umali

CRFA awards 2023 outstanding performers

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.