Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

TEVETA yati aliyense atha kuchita ntchito zamanja

Bungwe la Technical Entrepreneurial Vocational and Education Training Authority (TEVETA) likulingalira zolimbikitsa ndondomeko yofuna kuti maphunziro a ntchito za manja afikire anthu onse.

Wapampando wa bungweli, a Pyoka Tembo, amayankhula izi m’boma la Mulanje pamene amapereka malo ophunzirapo ntchitoyi otchedwa Ndanga, amene anawakonzanso atawonongeka ndi namondwe wa Anna ndi Gombe.

A Tembo anati achinyamata okhawo a luso ndi omwe angakwanitse kuthandidzira pa chitukuko chadziko lino.

M’modzi mwa amene watsiliza maphunziro a ulimi wa nkhumba, a Mary Maseko, anati maphunziro awo awapatsa kuthekera koti apeze phindu loyenelera mu ulimi wawo.

Pa mwambowu, TEVETA inaperekanso masitifiketi kwa anthu 125 omwe atsiriza maphunziro a ntchito zamanja monga zomangamanga, zaulimi wa nkhumba ndi luso losoka zovala.

 

Related posts

Chakwera concedes defeat, congratulates Mutharika

Romeo Umali

Parliamentarians urged to push for increased health allocation for women, children

Rabson Kondowe

REIAMA decries labour importation in energy sector

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.