Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

President Chakwera wati atsogoleri a mipingo ali ndi ntchito yayikulu

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera, wati atsogoleri amipingo ali ndi ntchito yaikulu yothandiza kupititsa patsogolo ntchito zachitukuko m’dziko muno.

Dr Chakwera alankhula izi pamene anali nawo pamwambo wa mapemphero pa mpingo wa Monkey Bay Assemblies of God m’boma la Mangochi.

“Inu atsogoleri a mipingo ndi amene dziko likudalira pachitukuko. Kupatula utumiki, tikudaliranso inu kutenga gawo polimbikitsa asungwana kupita patsogolo ndi maphunziro awo,” iwo anatero.

Mtsogoleri wadziko linoyu, amene analinso pamodzi ndi Madam Monica Chakwera, walimbikitsa a Khristu onse a mpingowu kuti akhale olimbikitsa umodzi muzochita zawo.

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Asilikali agwira nzika 276 zozembetsedwa zaku Ethiopia

Beatrice Mwape

Mw geared to end Cholera by 2030

Lonjezo Msodoka

Khonsolo ikufuna ndalama za chitukuko zidzibwera motsata ndondomeko

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.