Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

President Chakwera wati atsogoleri a mipingo ali ndi ntchito yayikulu

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera, wati atsogoleri amipingo ali ndi ntchito yaikulu yothandiza kupititsa patsogolo ntchito zachitukuko m’dziko muno.

Dr Chakwera alankhula izi pamene anali nawo pamwambo wa mapemphero pa mpingo wa Monkey Bay Assemblies of God m’boma la Mangochi.

“Inu atsogoleri a mipingo ndi amene dziko likudalira pachitukuko. Kupatula utumiki, tikudaliranso inu kutenga gawo polimbikitsa asungwana kupita patsogolo ndi maphunziro awo,” iwo anatero.

Mtsogoleri wadziko linoyu, amene analinso pamodzi ndi Madam Monica Chakwera, walimbikitsa a Khristu onse a mpingowu kuti akhale olimbikitsa umodzi muzochita zawo.

Olemba: Owen Mavula

Related posts

World Bank tips Malawi on economic recovery

Rabson Kondowe

Dedza DC establishes bursary committees to enhance support for students

Alinafe Mlamba

Wanderers, Bullets in second-spot showdown

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.