Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local Local News Nkhani

Polisi yadandaula ndi zilango zofewa pa milandu yoononga chilengedwe

Mkulu wa apolisi m’chigawo cha kum’mwera mbali ya ku mvuma, a Noel Kayira, ati zigamulo zomwe mabwalo ena a milandu akupereka pa milandu yoononga chilengedwe zikukolezerabe m’chitidwe oyipawu chifukwa zikumakhala zofewa.

Izi zikudza pamene anthu amene akumawapeza olakwa monga omwe akusakaza chilengedwe m’phiri la Michiru m’boma la Blantyre akumalamulidwa kuti apereke chindapusa cha K20,000 yokha.

A Kayira amayankhula m’malo mwa mkulu wa apolisi m’dziko muno, a Merlyne Yolamu, pa mwambo okambirana za lamulo latsopano lomwe likupereka chigamulo chokhwima kwa anthu okuba zipangizo zamagetsi.

Iwo anapempha mabwalo a milandu kuti lamuloli aligwiritse bwino ntchito pomapereka zigamulo zokhwima kwa amene apezeka olakwa.

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Chakwera departs Maputo for 44th SADC Heads of State Summit in Harare

Alinafe Mlamba

Female MSCE top performers to be awarded

Romeo Umali

Communities vandalise investor’s K450M property

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.