Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Osagwiritsa ntchito imfa ya malemu Dr Chilima pa zifukwa za ndale’

Gulu lomwe likuzitcha ‘Mbadwa Zokhudzidwa’ lapempha anthu a ndale kuti asiye kugwiritsantchito imfa ya Dr Saulos Chilima pofuna kumema anthu kuti adziwakonda.

M’busa Thoko Banda, amene ndi m’modzi mwa akuluakulu a gululi amayankhula izi loweruka mu mnzinda wa Lilongwe ndipo anauza a Malawi kuti asiye kukhulupilira mabodza andale oterewa.

Mkulu winanso wa bungweli, a Billy Malata, anachenjeza a Malawi amene akufalitsa uthenga wabodza pa masamba a mchezo kuti azagamulidwa mlandu akawapeza.

A Malata analimbikitsanso chipani cha Malawi Congress (MCP) kuti chisachite ndale zonyoza.

 

Related posts

Maize prices drop in September

Romeo Umali

JZU’S  LEGACY INDELIBLE

McDonald Chiwayula

TRADE IN A DRIVE TO BAIL OUT FARMERS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.