Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Ntchito zokhudza maulendo wapa ndege sizinaime’

Mkulu wa nthambi yoona zamaulendo apa ndege m’dziko muno (Department of Civil Aviation), a Vetrus Francis Dziwe, wati ntchito za maulendo apa ndege zikuyenda bwino popanda chilichonse chopinga.

Poyankhula ndi MBC Digital, a Dziwe ati apitiriza kuonetsetsa kuti zonse zili m’chimake.

“Ndege ya mammawa yopita ku Republic of South Africa yapita kalekale, apa anthu akukonzekera (ya 10 koloko) yopita ku Lusaka m’dziko la Zambia choncho palibe chopinga,” anatero a Dziwe.

Ndipo ena mwa akuluakulu aku nthambi yoona za anthu olowa ndi kutuluka m’dziko muno atsimikiza kuti malo onse anthambiyi, kuphatizapo mzipata zolowera mdziko muno, ntchito zikuyenda bwino lomwe.

Mmasamba amchezo mwakhala mukuzungulira kalata yokhala ngati kuti  anthu ena ogwira ntchito ku Immigration amamema anzawo wogwira ntchito ku dipatimentiyi  kuti lero Lachinayi pa 6 June ayambe  kunyanyala ntchito zawo.

Ndipo chikalata china  chikuonetsanso kuti unduna waza chitetezo cha m’dziko, omwe umayang’anira nthambiyi, wadzudzula mchitidwewu.

Malinga ndi chikalatacho, chomwe wasaina mlembi ku undunawu a Steven Kayuni, zomwe  ma ofesalawo amafuna kuchita ndikulakwira malamulo kamba koti sadatsatire ndondomeko kukhala nthambi yaza chitetezo.

Related posts

Giboh Pearson wapulumuka ku ngozi

Romeo Umali

Preparations for Karonga-Chitipa cultural festival on track

Romeo Umali

Wittika’s murder case adjourned

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.