Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local Music News Nkhani

Giboh Pearson wapulumuka ku ngozi

Katswiri oyimba amene amachokera m’boma la Phalombe, Giboh Pearson, wapulumuka pa ngozi ya galimoto yomwe wachita pomwe amapita ku phwando la msangulutso ku Bangwe mu mzinda wa Blantyre.

Malinga ndi Pearson, chiwongolero komanso mabuleki agalimoto lake zinasiya kugwira ntchito, zomwe zinachititsa kuti akanike kuwongolera galimotoli ndipo linatembenuzika.

“Ndachita ngozi koma ndili bwino,” watero Giboh patsamba lake la mchezo.

Pangoziyi palibe wavulala.

 

Related posts

GOVERNMENT HAILS NRWB FOR USING SOLAR ENERGY

MBC Online

Increase safety net allocations – World Bank

Rabson Kondowe

Activists push for Reusable Sanitary Pads to combat period poverty

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.