Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Ntchito yoponya voti ili mkati ku ward ya Mwasa

Ntchito yoponya voti pachisankho chapadera chosankha khansala wa dera la Mwasa ili mkati m’boma la Mangochi.

Pamene imakwana 5:30 m’mawa, anthu ochuluka anayamba kufika pamalo oponya voti pa sukulu ya pulaimare ya St St Augustine 3.

Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) likuchititsa chisankho chapaderachi potsatira imfa ya yemwe anali khansala waderali malemu Edna Yusuf Jose m’chaka cha 2022.

Pakadali pano, Komishonala wa bungwe la MEC, a Richard Chapweteka, ati bungweli ndi lokhutira ndi momwe ntchito yoponya voti yayambira.

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MEC ionjezera masiku m’gawo loyamba la kalembera

Austin Fukula

Major Flora Selemani-Ngwilinji’s inspirational story

MBC Online

MRA collects K660BN in 2024/25 first quarter

Earlene Chimoyo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.