Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Ntchito yoponya voti ili mkati ku ward ya Mwasa

Ntchito yoponya voti pachisankho chapadera chosankha khansala wa dera la Mwasa ili mkati m’boma la Mangochi.

Pamene imakwana 5:30 m’mawa, anthu ochuluka anayamba kufika pamalo oponya voti pa sukulu ya pulaimare ya St St Augustine 3.

Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) likuchititsa chisankho chapaderachi potsatira imfa ya yemwe anali khansala waderali malemu Edna Yusuf Jose m’chaka cha 2022.

Pakadali pano, Komishonala wa bungwe la MEC, a Richard Chapweteka, ati bungweli ndi lokhutira ndi momwe ntchito yoponya voti yayambira.

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Land dispute case adjourned to September

MBC Online

Alimi olimbikira akondweretsa mayi Mia

Arthur Chokhotho

Polymed Sacco posts K200 million profit

Jeffrey Chinawa
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.