Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Ntchito yodinda ma pasipoti yayambiranso ku Mzuzu

Nthambi yoona zolowa ndi kutukuka mdziko muno ya Immigration yalengeza zakuyambanso kwa ntchito yodinda ndikupereka ziphaso zoyendera mchigawo chakumpoto.

Malinga ndi chikalata chomwe wasayinira ndi mneneri kunthambiyi a Wellington Chiponde, kuyambira lolemba pa 29 July anthu ofuna mapasipoti tsopano atha kufika ku Mzuzu dongosolo lonse loyenerera kuti akhale ndi chiphasochi.

Nthambi ya Immigration yakhala isakudinda ziphaso zoyendera kwanthawi ndipo yayamikira anthu kaamba kakudekha kwawo panthawiyi.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Zokonzekera msonkhano wapachaka wa Surveyors Institute of Malawi zili mchimake

Paul Mlowoka

Mfumu Ngokwe yayamika magulu akufuna kwabwino

MBC Online

Lipoti lokhudza ngozi ya ndege ku Chikangawa yatuluka

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.