Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MUST ichititsa chionetsero cha chikhalidwe

Sukulu ya ukachenjede ya MUST m’boma la Thyolo yakonzeka kuchititsa chionetsero cha chikhalidwe, kafukufuku ndi luso cha chaka chino, kuchokera pa 4 mpaka pa 5 October. 

Ichi chikhala chionetsero chachiwiri kuchoka pomwe anakhazikitsa zochitikazi chaka chatha.

Malinga ndi mkulu wa zamaphunziro a chikhalidwe ku MUST, Atikonda Mtenje-Mkochi, chiyembekezo chawo ndi chakuti chionetserocho chithandiza kuti luso lomwe likugwirizana ndi chikhalidwe likhale laphindu pa chitukuko cha dziko lino.

Mwazina, pa chionetserocho padzakhala zoimbaimba za akatswiri monga Jetu.

Mutu wa chionetserocho chaka chino ndi Chikhalidwe: Nsanamira ya Chitukuko.

Related posts

UTM yapempha mgwirizano pa nthawi ya maliro

Rabson Kondowe

Scorchers first defeat at COSAFA: a distraction from WAFCON?

Romeo Umali

Phindu la Illovo latsika mu miyezi isanu ndi umodzi

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.