Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MUST ichititsa chionetsero cha chikhalidwe

Sukulu ya ukachenjede ya MUST m’boma la Thyolo yakonzeka kuchititsa chionetsero cha chikhalidwe, kafukufuku ndi luso cha chaka chino, kuchokera pa 4 mpaka pa 5 October. 

Ichi chikhala chionetsero chachiwiri kuchoka pomwe anakhazikitsa zochitikazi chaka chatha.

Malinga ndi mkulu wa zamaphunziro a chikhalidwe ku MUST, Atikonda Mtenje-Mkochi, chiyembekezo chawo ndi chakuti chionetserocho chithandiza kuti luso lomwe likugwirizana ndi chikhalidwe likhale laphindu pa chitukuko cha dziko lino.

Mwazina, pa chionetserocho padzakhala zoimbaimba za akatswiri monga Jetu.

Mutu wa chionetserocho chaka chino ndi Chikhalidwe: Nsanamira ya Chitukuko.

Related posts

2025/26 national budget aligns with MW2063 — NPC

Romeo Umali

Nsanje commemorates Day of the African child

Romeo Umali

Female police officers in Lumbadzi urged to lead fight against GBV

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.