Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

MRCS yapereka madzi a m’mipopi ku Karonga

Bungwe la Malawi Red Cross Society (MRCS) lapereka madzi a m’mipopi kwa anthu a m’dera la mfumu yayikulu Mwirang’ombe m’boma la Karonga pofuna kulimbikitsa ukhondo.

Madziwa ndi odalira mphamvu ya dzuwa ndipo pali mipopi 16 yomwe yayikidwa m’malo osiyanasiyana.

M’modzi mwa akuluakulu abungweli, a Dan Nyirenda, ati madziwa afikira mabanja 480 kuphatikizapo sukulu ya pulayimale ya Ngara, chipatala cha ching’ono cha m’deralo komanso malo ochitira malonda.

Yemwe anayimira Bwanamkubwa wa bomali, a Yaz Nyirenda, anati anthu m’derali amavutika kaamba kosowa madzi abwino ndipo thandizoli lithetsa vutoli.

M’modzi mwa amayi okhala m’mudzi mwa agulupu a Muyeleka, a Watipaso Simeza, anathokoza chitukukochi.

“Poyamba timatenga madzi kunyanja komwe ndi kutali komanso madziwo sanali awukhondo,” a Simeza anatero.

Chifukwa chosowa madzi awukhondo, chaka chatha chokha anthu 63 akhala akugwidwa ndi nthenda ya Cholera ndipo asanu ndi awiri anafa ndi nthendayi.

Olemba: George Mkandawire

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Villages in T/A Tsabango in need of safe water

MBC Online

Kambira Secondary School opened

MBC Online

Mediation efforts to end truck drivers’ strike underway

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.