Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

Mavenda ku 25 atseka sitolo ya m’mwenye kaamba kotsitsa mitengo

Ochita malonda (Mavenda) aku Nsungwi ku Area 25 mu mzinda wa Lilongwe atseka shop ya m’mwenye wina yemwe amadziwika bwino ndi dzina lakuti Farook ponena kuti wakhala akulowetsa malonda awo pansi.

Anthu okhudzidwa ati mkuluyu amatsitsa kwambiri mitengo ya katundu wawo.

A Albert Zuwawo, omwe amagulitsa zipangizo za katundu osiyanasiyana (Hardware) ati ndi povuta kuti alimbane ndi a Farook popeza iwo ali ndi mpamba ochepa.

“Pa chifukwa ichi, tatseka shopuyo kuti iye apite komwe kuli olimbana naye pa chuma ife za ziwawa ayi,” anatero a Zuwawo.

Ochita malonda pa zokambirana.

Wapampando wa msikawu, a John Mbumba, ati iwo amakanika kuti alowelerepo popeza m’mwenyeyo amawapatsa ndalama ngati yowatsekera pakamwa, yomwe ati imalowa ku thumba la msika komanso katundu wina amapanga yekha.

Mlembi wa ku unduna woona za malonda, a Christina Zakeyu, auza MBC Digital kuti padakali pano iwo adakafufuzabe za nkhaniyi.

Poyankhulapo, a Kate Kamwangala, omwe ndi mtsogoleri wa bungwe la Black Indigenous Business Network, ati ndi kofunika kuti ochita malonda a ang’ono adzikhala otetezedwa pofuna kuti athandize kukweza chuma cha dziko lino.

Msika wa Nsungwi anautsekula m’chaka cha 2002 mu mzinda wa Lilongwe.

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Chakwera arrives in Mangochi

MBC Online

Maize prices drop in September

Justin Mkweu

Media key in economic growth – Oxfam

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.