Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani Sports

Mankhwala oletsedwa mmasewero atha kuononga mbiri ya dziko – MADO

Bungwe lomwe limawona za mchitidwe ogwiritsa ntchito mankhwala osaloledwa mmasewero la Malawi Anti-Doping Organisation (MADO) lati kugwiritsa ntchito mankhwala oletsedwa mmasewero kuli ndikuthekera koipitsa mbiri yadziko.

Mlembi wa bungweli, a Leonard Sharra, anena izi mu mzinda wa Lilongwe pomwe bungweli likuphunzitsa atolankhani komanso atsogoleri ndi alembi anthambi zamasewero mdziko muno zokhudza momwe angathanirane ndi mchitidwewu.

“Ngati wina atayezedwa nkupezeka kuti amagwiritsa ntchito mankhwala kuti awonjezere mphamvu ndikupeza chipambano, zidzaononga mbiri yamasewero komanso dziko,” anatero a Sharra.

Mmawu ake mkulu owona zamasewero ku unduna wa zamasewero, a Jameson Ndalama, ayamikira MADO kaamba ka mamphunzirowa ndipo ati kuphwanya malamulo kukhala kusamvera chabe koma aphunzitsidwa zonse zoyenelera kutsatira pamasewero.

Malinga ndi wapampando wa MADO, a James Mwenda, bungweli lalandira ndalama zokwana pafupifupi $20,000 kuchokera ku komiti yoona za masewero pa dziko lapansi kuti zithandize kufalitsa uthenga okhudza kugwiritsa ntchito mankhwala ndi njira zosaloledwa mmasewero.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Wina wapambananso!

Jeffrey Chinawa

Mlimi apata mphoto ya K10 million

Simeon Boyce

Kukhala madyelero pomwe asilamu akukondwelera Eid

Simeon Boyce
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.