Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MACRA ikufuna mtengo wa ‘smartphone’ utsike

Bungwe la Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) lati likufuna mitengo ya ma ‘smartphone’ kapena kuti lamya zammanja zomwe  ziri ndi  ‘internet’ zikhale zotsika mtengo mdziko muno.

Mkulu wa bungweli a Daud Suleman wati kukwera mtengo kwa lamya zammanjazi  kukuchititsa kuti a Malawi ochepa okwana 1 million okha akhale ndi mwayi ogwiritsa ntchito zinthu zomwe zikupezeka pa makina atsopano a ‘internet’.

Apa iwo ati kukwera mtengoku kukuchitika chifukwa choti lamyazi amachita kuyitanitsa kuchokera mayiko akunja ndikuti zikamafika kuno zimakwera mtengo kwambiri.

“Poyesetsa kuti lamyazi zitsike mtengo tili ndi chikonzero chothandizana ndi makampani ena kuti tidziyitanitsa zipangizo zopangira malamyawa kuti tidzilumikiza konkuno ndicholinga choti mitengo itsike,” anatero a Suleman.

 

Wolemba: Henry Haukeya

Related posts

Police officer donates school uniform in Lilongwe

Romeo Umali

Youths are agents of Peace — YONECO

Romeo Umali

AGCOM ikutukula alimi

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.