Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local Music News

Lucius anali bwenzi lama Rasta — Ras Jonah

Yemwe amakhala pafupi ndi nyumba ya malemu “soldier” Lucius Banda m’boma la Balaka, Ras Jonah, yemwe dzina lake lenileni ndi Ronald Chigwale, wati mu nyimbo zake zambiri, malemu “soldier” mumakhalanso uthenga umene ma Rasta amakonda kupereka, monga kulakhulira anthuopondelezedwa, kulimbikitsa anthu kukhala olimbikira pa ntchito komanso kulimbikitsa chikondi.

Ras Jonah, yemwenso ndi oyimba, wati m’chaka cha 2002, malemu Lucius Banda anathandiza msonkhano wawo wawukulu wa ma Rasta ku Salima, kumene kunaabweranso oyimba akunja pamwambo wa zoimbaimba, umene ndalama zonse anazipeleka kukathandizira chilinganizochi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

SUSU IN MALAWI

Mayeso Chikhadzula

South West Region sees surge in homicide, theft cases

Romeo Umali

Three die, four seriously injured in Mangochi road accident

Davie Umar
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.