Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

FAM ikusaka ma passport a Flames

Mkulu ofalitsankhani komanso kuyendetsa mipikisano ku bungwe la FAM, a Gomezgani Zakazaka, ati ntchito yofufuza ma passport a osewera atimu ya Flames omwe asowa m’dziko la Mali ikupitilirabe.

Malinga ndi malipoti, m’modzi mwa akuluakulu a timuyi anaiwala ma passport amenewa mu taxi yomwe anakwera.

Malawi ili m’dziko la Mali pomwe usiku uno ikuyembekezeka kuti isewele ndi timu ya Burkina Faso mu masewero a mu ndime yodzigulira malo ku mpikisano wa AFCON.

Kanema za MBC komanso wailesi ya Radio 2 fm zilengezera masewero wa omwe ayambe 9 koloko usiku uno.

 

Olemba: Amin Mussa

Related posts

Malawi excels in the fight against malaria — Baloyi

MBC Online

Remnant Lions Theatre Group to premier “Belinda”

Rabson Kondowe

Mpinganjira expresses gratitude for Chakwera’s visit to IBCC

Secret Segula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.