Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

FAM ikusaka ma passport a Flames

Mkulu ofalitsankhani komanso kuyendetsa mipikisano ku bungwe la FAM, a Gomezgani Zakazaka, ati ntchito yofufuza ma passport a osewera atimu ya Flames omwe asowa m’dziko la Mali ikupitilirabe.

Malinga ndi malipoti, m’modzi mwa akuluakulu a timuyi anaiwala ma passport amenewa mu taxi yomwe anakwera.

Malawi ili m’dziko la Mali pomwe usiku uno ikuyembekezeka kuti isewele ndi timu ya Burkina Faso mu masewero a mu ndime yodzigulira malo ku mpikisano wa AFCON.

Kanema za MBC komanso wailesi ya Radio 2 fm zilengezera masewero wa omwe ayambe 9 koloko usiku uno.

 

Olemba: Amin Mussa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Social Cash Transfer Programme will reach vulnerable people’

Olive Phiri

Chakwera visits Kamuzu Tree in Chikangawa

MBC Online

MFC champions sustainable fertilizer usage in Malawi

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.