Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Dr Chilima anali wosayang’ana zigawo – Kaliati

Mlembi wamkulu wa chipani cha UTM a Patricia Kaliati wati malemu Dr Saulos Chilima anaonetsa chitsanzo chabwino potumikira dziko lino modzipereka posayang’ana zigawo.

A Kaliati ayankhula izi ku Mzuzu pa msonkhano wokumbukira malemu Dr Chilima yemwe anali mtsogoleri wa chipani cha UTM komanso wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino.

Iwo ati Dr Chilima anaikapo mtima pofuna kusintha dziko lino komanso kuti achinyamata akhale mzika zodalirika.

Atsogoleri ena a chipani cha UTM anati chipanichi chipitilira kukhala champhamvu pofuna kukwaniritsa masomphenya a yemwe anali mtsogoleri wachipanichi Dr Saulos Chilima.

Dr Chilima pamodzi ndi anthu ena asanu ndi atatu anafa pa ngozi ya ndege ku Chikangawa m’boma la Mzimba pa 10 June 2024.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Bambo wazaka 70 akhala kundende zaka 14 chifukwa chogwililira

Davie Umar

Airtel Top 8 iyamba pa 14 September

Romeo Umali

Agwetsa sitolo zomangidwa malo osavomerezeka

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.