Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani Sports

Blue Eagles yatsala ndi ma poyinsi atatu kuti ibwerere mu super league

Timu ya Blue Eagles yalimbikitsa mwayi wake obweleranso mu ligi yaikulu ya TNM pomwe yagonjetsa Ekas Freight Wanderers ndi zigoli zinayi kwa zero pabwalo la Airport Development Limited munzinda wa Lilongwe.

Ganizani James, Laurent Banda, Tonic Vivuyi ndi Miccium Mhone ndiomwe anamwetsa dzigolizi zomwe zapangitsa kuti timuyi idzitsogola ndi mapoinsi 12. Eagles ili ndi ma poyinsi 48 itasewera masewero 18 pomwe Villa yomwe ndiyachiwiri ili ndi ma poyinsi 36 itasewera masewero 17.

Izi zikutanthauza kuti  Eagles yomwe siinangonjepo mu ligi ya Chipiku ikungofunika mapoyinsi atatu pamasewero anayi omwe yatsala nawo,  Koma mphuzitsi wa timuyi Eliya Kananji wati anyamata ake satayirira  chifukwa ulendo wobwelera mu Super League sunatheke.

Zotsatira zamasewero ena omwe aseweredwa lero, Armour Battalion yagonjetsa Wimbe United 3 – 0, St Gabriel Zitha yathambitsa Extreme 3 – 0, pomwe Mitundu Baptist yagonja ndizigoli ziwiri  pakhomo ndi timu ya Mbadzi United.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Nadolo and Chirwa triumph in 6th Blantyre 42.195 Kilometre race

MBC Online

Police to deploy intelligence-driven operation

Chisomo Break

Promised Land Foundation brings relief with potable water system

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.