Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi ku Mangochi amanga Boika atam’peza ndi chida choopsya

Apolisi ku Mangochi amanga a Boika Sabiti, 48, atawapeza ndi chida choopsya chopangidwa ndi zitsulo zosongoka komanso zokuthwa.

Ofalitsa Nkhani pa Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, ati a Sabiti adawapeza ndi chidachi pa malo omwela mowa m’boma la Mangochi.

“Tinawuzidwa ndi anthu ena akufuna kwabwino kuti a Sabiti akuyenda ndi chida choopsa chomwe anasunga m’chikwama chomwe amayenda nacho, ndipo ife apolisi tidathamangira kwa Mtalimanja komwe tinawapeza nacho,” a Daudi anatero.

Sabiti, amene amachokera m’mudzi wa Mapira ku Mangochi, ndi kabwerebwere kundende ndipo akaonekela kukhothi kukayankha mulandu opezeka ndi chida chowopsa.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Local ICT firm offers custom-made software

MBC Online

EXECUTIVE MANAGEMENT PLACEMENT: DIRECTOR OF NEWS AND CURRENT AFFAIRS (READVERTISED)

MBC Online

KALINDO’S WARRANT OF ARREST SUSPENDED

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.