Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local Local News Nkhani

Aliyense atenge gawo posamala misika — Khonsolo ya Lilongwe

Khonsolo ya Mzinda wa Lilongwe yapempha mzika zake kukhala adindo pa ntchito yosamala misika yosiyanasiyana ya mumzindawu.

Mfumu ya mzinda wa Lilongwe, a Esther Sagawa, ndi imene yapereka pempholi pamene khonsoloyi imalandira zipangizo kuchokera ku kampani ya Waste Advisers, imene yapereka ndi kuyika malo otayola zinyalala (waste bins) okwana 100.

A Sagawa anati ndikofunika kuti anthu ayambe kuzindikira udindo wawo komanso kutenga nawo gawo losamalira misikayi popewa kutaya zinyalala mwachisawawa kuti idzikhala yaukhondo.

Mkulu oyendetsa ntchito za Waste Advisers, a John Chome, anati ndi khumbo lawo kuona misika ndi mizinda ya dziko lino ili yosamalika komanso yochititsa kaso.

Ntchitoyi ayikhazikitsanso m’zigawo zonse za dziko lino ndipo ndiya ndalama zokwana K12 million, pansi pa mutu wakuti ‘Khalani aukhondo, tayani zinyalala zanu moyenera’.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CHAKWERA EXPERIENCES MAKANJIRA ROAD’ ROUGH TERRAIN

MBC Online

Thandizani mpira wa m’maboma — CRFA

Paul Mlowoka

Chakwera launches dry spell, floods response appeal

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.