Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local News

Alimi apempha Dr Chakwera kuti awathandize kupeza misika mosavuta

Bungwe la alimi m’dziko muno la Farmers Union of Malawi (FUM) lapempha mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, kuti awathandize kupeza misika mosavuta.

Mtsogoleri wa bungweli, a Maness Nkhata, amalankhula izi ku nyumba yaboma munzinda wa Lilongwe kumene iwo amakumana ndi Dr Chakwera.

Mwa zina, a Nkhata anati anakakonda kuti bungwe la National Food Reserve Agency (NFRA) likhale ndi makina owumitsira chimanga chifukwa chimanga chambiri chikumabwezedwa.

Iwo anayamikiranso mtsogoleri wa dziko lino poikirapo mtima pokweza ntchito za ulimi m’dziko muno, kuphatikizapo kuyambitsa ulimi wa minda yaikulu ya Mega Farms.

A Nkhata anapemphanso kuti pakhale mwayi oti alimi adzipeza mpata wopatsidwa ngongole kuchokela ku bungwe la National Economic Empowerment Fund (NEEF).

Alimi osiyanasiyana ochokera m’maboma onse m’dziko muno ndi amene anakumana ndi Dr Chakwera ku Lilongwe, pansi pa bungwe la FUM.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Msilikali Sacco AGM approves K156M dividends payout

Yamikani Simutowe

Chakwera calls for collaboration among African countries for improved farmer welfare

Beatrice Mwape

Nduna yazofalitsa nkhani ipereka lipoti la ngozi ya ndege ya Chichewa

Olive Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.