Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports

FAM ilowerere pakuvulazidwa kwa Wongani Lungu — Bullets

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yati ikufuna kuti bungwe la Football Association of Malawi lilowerere pazomwe zinachitika pamasewero awo ndi timu ya MAFCO lamulungu lapitali pabwalo la Kamuzu.

Osewera wa Bullets Wongani Lungu anapondedwa mwadala ndi osewera a MAFCO, Vitumbiko Phiri, Blessings Chandiyang’ana ndi Duncan Mwale m’masewero amu super ligi.

Polankhula ndi atolankhani, presidenti watimuyi, Konrad Buckle wati ndiokhumudwa kwambiri zomwe zinachitikazi ndipo adindo akuyenera abweretse chigamulo chankhaniyi mwansanga.

Lungu akhala pafupifupi sabata imodzi osasewera mpira kamba kakuvulala pamasewerowa.

Mkulu wa Bullets, Albert Chigoga wapemphanso bungwe la oyimbira masewero ampira wa miyendo m’dziko muno kuti aunikilenso zankhaniyi.

Olemba : Praise Majawa

Related posts

Mlingo wa kukwera mtengo kwa zinthu (inflation) watsika mu February

Rabson Kondowe

Apereka chindapusa pa milandu yosakaza chilengedwe

Mayeso Chikhadzula

Drones in the Air at Chikangawa

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.