Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MCP ikufuna zipani zidzichita misonkhano mwaufulu

Chipani cha Malawi Congress (MCP) chati ndikofunika kuti chipani chilichonse m’dziko muno chidzilemekeza ufulu wa demokalase komanso kuchita misonkhano mwa mtendere ndi bata.

Mlembi wamkulu wa MCP, a Richard Chimwendo Banda, amayankhula izi Lachisanu mu nyumba ya malamulo munzinda wa Lilongwe pamene amayankha pempho la mtsogoleri wa aphungu otsutsa boma, a George Chaponda.

A Chaponda anapempha boma kuti lilowerelepo kuti pasadzakhale zipolowe pa msonkhano umene akonza a chipani cha Democratic Progressive munzinda wa Mzuzu komanso wa MCP ku Ekwendeni m’boma la Mzimba.

A Chimwendo Banda anati chipani chawo sichifuna zipolowe ndipo anati palibe vuto kuti zipani ziwiri zichititse msonkhano kaamba kakuti malo amene kukachitikire misonkhanoyo ndi otalikana makilomita 21.

Related posts

Dr Chakwera ati akufuna kubwezeretsa zomwe zinaonongeka

Romeo Umali

Environmental Conservation efforts praised in Dedza

Romeo Umali

Maranatha Academy, Sharda University host education fair

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.