Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MCP ikufuna zipani zidzichita misonkhano mwaufulu

Chipani cha Malawi Congress (MCP) chati ndikofunika kuti chipani chilichonse m’dziko muno chidzilemekeza ufulu wa demokalase komanso kuchita misonkhano mwa mtendere ndi bata.

Mlembi wamkulu wa MCP, a Richard Chimwendo Banda, amayankhula izi Lachisanu mu nyumba ya malamulo munzinda wa Lilongwe pamene amayankha pempho la mtsogoleri wa aphungu otsutsa boma, a George Chaponda.

A Chaponda anapempha boma kuti lilowerelepo kuti pasadzakhale zipolowe pa msonkhano umene akonza a chipani cha Democratic Progressive munzinda wa Mzuzu komanso wa MCP ku Ekwendeni m’boma la Mzimba.

A Chimwendo Banda anati chipani chawo sichifuna zipolowe ndipo anati palibe vuto kuti zipani ziwiri zichititse msonkhano kaamba kakuti malo amene kukachitikire misonkhanoyo ndi otalikana makilomita 21.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chakwera reveals ambitious plan for cervical cancer centres

Alinafe Mlamba

Malawi Digital Network revolutionises academic research at MUBAS

MBC Online

Scorchers lero imwemwetera

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.