Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

‘Odwala sakumadya mokwanira’

Komiti ya nyumba ya malamulo yoona zaumoyo yati zipitala zambiri zikulephera kupereka chakudya mokwanira kwa odwala chifukwa cha kuchepekedwa kumbali ya ndalama.

Wapampando wa komitiyi, a Matthews Ngwale, ananena izi m’nyumbayi pamene amapereka lipoti lokhudza kaperekedwe ka chakudya kwa odwala m’zipatala za m’dziko muno.

A Ngwale anati aphungu a komiti yawo anayendera zipatala za maboma a Thyolo, Balaka, Dowa, Rumphi komanso Ntcheu pamene amafuna kukaona m’mene nkhani yopereka chakudya kwa odwala ikuyendera.

Chipatala cha Mzimba chokha akuti ndi chimene chikukwanitsa kupereka chakudya katatu patsiku.

Komitiyi yapempha boma kuti lidzipereka ndalama zokwanira komanso mu nthawi yake kuti mavutowa achepe.

Related posts

School Feeding Programme can combat malnutrition — MoE

Romeo Umali

Wakabaza waphula K200 million ya BetPawa

Romeo Umali

Jetu hypes Charisma’s City Heist event

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.