Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

‘Masewero ndi njira yofalitsa uthenga wa uchembere wabwino’

Masewero ndi njira yabwino yofalitsira mauthenga a uchembere wabwino komanso kudziwa za ma ufulu a achinyamata pa nkhani zogonana komanso banja, bungwe la Umunthu Foundation latero.

Mkulu wa bungweli, a David Odali, anena izi pa mkumano ndi achinyamata osewera mpira miyendo komanso wa manja ndi aphunzitsi a matimu 20 pa bwalo lamasewero a Mpira, ku Chiwembe mu mzinda wa Blantyre.

Iwo anati achinyamata amakonda kupezeka pa malo pamene pa kuchitika masewero, kotero pakufunika kuwagwiritsa ntchito pofalitsa mauthenga otere.

Pa mkumanowu, bungwe la Umunthu Foundation linaperekanso mipira ku matimuwa.

 

Related posts

MOTHER, DAUGHTER DROWN IN RIVER

Rabson Kondowe

Education ministry eyes ODeL expansion as learner numbers rise

Rabson Kondowe

Ntchito yopopa madzi mu nyanja ya Malawi ichepetsa vuto la madzi ku Dowa – Chakwera

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.