Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Alimi aguliretu mbewu zoyenera — SeedCo

Kampani yopanga mbewu ya SeedCo yalangiza alimi kuti aguliretu mbewu zovomerezeka nyengo ya dzinja isanafike.

A Dennis Mdzalimbo, omwe amaona zamalonda  Ku kampaniyi  anati kugula mbewu zovomerezeka kumathandiza kuti ulimi ukhale waphindu.

Iwo amayankhula izi pa msonkhano omwe anachititsa ndi anthu komanso makampani omwe amagulitsa mbewu ochokera ku chigawo cha kumpoto.

A Mdzalimbo alangizanso alimi kuti adzitsatira ulangizi wa zanyengo kuti adzibzyala mbewu zogwirizana ndi momwe mvula ikugwera.

Malingana ndi akatswiri a zanyengo, madera ena m’chigawo cha kumpoto mugwa mvula yocheperako chaka chino kamba ka mphepo yotchedwa La Nina.

 

Olemba: Chimwemwe Milulu

Related posts

Self Help Africa winds up mission in Dedza

Romeo Umali

Malawi conducts first study on Parkinson’s Disease

Romeo Umali

Human First reaches out to 17 million people 30 years

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.