Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Zaka zitatu pogulitsa makala mosatsata lamulo

Khothi la Magistrate mu mzinda wa Blantyre la lamula kuti abambo atatu akagwire ukayidi kwa zaka ziwiri komanso chaka ndi theka kaamba kopezeka olakwa pochita malonda ogulitsa makala opanda chiphaso komanso kuzembetsa zinthu za munkhalango.

Popereka chigamulo, Magistrate Godfrey Balaka anati zilango zonsezi ziyendera limodzi pofuna kuti anthu ena atengerepo phunziro ndipo mlanduwu adapalamula pa 17 April, 2024.

Nthambi za boma monga Police, ACB ndi nthambi ya zankhalango padakali pano zikugwira limodzi ntchito yothandiza kuteteza zachilengedwe.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Dziko la Malawi lili ndi mwai waukulu woonjezera Mphamvu zamagetsi

Mayeso Chikhadzula

MRA lauds editors’ role in highlighting national development

McDonald Chiwayula

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.