Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

President Chakwera akayendera ntchito zachitukuko kumpoto

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, lero anyamuka ku Lilongwe kupita mchigawo chakumpoto kumene akayendere ntchito zina zachitukuko.

Malinga ndi kalata imene wasayinira mlembi wamkulu mu ofesi ya President ndi  nduna zake, a Colleen Zamba, mwazina Dr Chakwera akakhala nawo pamwambo watsiku lokumbukira anthu amene adadzipereka kuti dziko lino likhale pa ufulu (Martyrs Day).

Mwambowu umakhalapo pa 3 March chaka chilichonse ndipo chaka chino tsikuli likhala pa lamulungu (Sunday).

Related posts

Journalist Chimgwede triumphs in Kasungu primaries

MBC Online

Number of children accessing HIV & AIDS services spikes in CZ

Romeo Umali

World Bank tips Malawi on economic recovery

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.