Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Zokonzekera msonkhano wapachaka wa Surveyors Institute of Malawi zili mchimake

Bungwe la Surveyors Institute of Malawi lati chilichonse chili mchimake pa zokonzekera za msonkhano wawo waukulu wapachaka umene uyambe pa 26 mpakana pa 27 mwezi uno.

Mlembi wamkulu wa bungweli, a Bernard Mleta, ndi amene amayankhula izi Lachiwiri masana atalandira thandizo la ndalama zokwana K3 million kuchokera ku kampani ya Property Solutions Limited.

A Mleta anayamikira kampaniyi kaamba ka thandizoli chifukwa laonetsa poyera kuti ali ndi chidwi chokweza ntchito zabungweli.

Mkulu wa Property Solutions, a Willy Mwawa, anati athandiza chifukwa akudziwa zakufunika kwa mwambowu komanso ngati membala wa bungweli, ndi udindo wawo kutero.

Kampaniyi imagwira ntchito younika kuchuluka ndi mlingo wa zinthu kapena malo m’dziko muno.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

POLICE RESCUE MINORS, ARREST DEFILERS IN NIGHT RAID

Patrick Kajusu

WLA HOLDS LEGAL CLINIC IN MCHINJI

McDonald Chiwayula

MDF calls for improved welfare of its retirees

Trust Ofesi
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.