Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Tabitha wakankha chikopa mogometsa mu February ku France

Katswiri wampira wamiyendo wadziko lino Tabitha Chawinga walandira mendulo ngati osewera mogometsa m’mwezi wa February 2024 mu ligi yayikulu ya mpira wa miyendo ya amayi m’dziko la France.

Chawinga anayamikira anzake amene amasewera nawo ku timu yake ya Paris Saint-Germain (PSG) Féminines,ponena kuti ndiwo apangitsa kuti apeze mphothoyi.

Msungwanayu akutsogola pa m’ndandanda wa omwetsa zigoli mu ligiyo, atamwetsa zigoli zakwana 13 pa masewero 17.

Aka ndi koyamba kuti katswiriyu alandire menduloyi.

 

Related posts

SCT gives hope to Cyclone Freddy survivors in Nsanje

MBC Online

Russia reaffirms commitment to Africa’s development through strategic partnerships

Yamikani Simtowe

GOVT APPOINTS NEW SFFRFM BOARD

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.