Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local News Nkhani

Pulezidenti wakale wa FAMA wafunira zabwino Mayi Kingston

Mtsogoleri wakale wa bungwe la Film Association of Malawi (FAMA), a Gift Sukali, wafunira zabwino atsogoleri atsopano amene bungweli lawasankha kumene.

A Sukali ati ndi okondwa ndi kuti akuchoka pampandowu atakwaniritsa zambiri monga kuwonetsetsa kuti anthu akudziwa zazisudzo zapakanema komanso kutha kupeza phindu kupyolera mmakanemawa.

Iwo ati ali ndi chikhulupiliro kuti utsogoleri watsopanowu ukwaniritsa masomphenya a FAMA ndi kupititsa patsogolo bungweli kuti lithe kupeza thumba loliyendetsera.

Mtsogoleri watsopano wabungweli ndi a Dorothy Kingston, mkazi wa katswiri oyimba Zeze. Iwowa akhala akutsogolera bungweli kwa zaka zinayi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi Beach Soccer takes on Burundi

Romeo Umali

Agriculture fair key in boosting market access for farmers – FAMSE

Chisomo Break

Madam Chakwera afika ku mwambo okumbukira tsiku la anthu achialubino

Eunice Ndhlovu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.