Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local Local News Nkhani

MRCS yamaliza kuthandiza okhudzidwa ndi namodwe Judy ku Phalombe

Bungwe la Malawi Red Cross Society (MRCS) lati lamaliza ntchito yogawa ndalama kwa mabanja amene anakhudzidwa ndi namondwe Judy m’boma la Phalombe m’chaka cha 2023.

Mabanjawa ndi oposa 1,000 ndipo alandira K140,000 komanso sopo ochapira ndi osambira banja lililonse.

M’modzi wa akuluakulu ku bungweli, a Leanord Maganga, ati ali ndi chikhulupiliro kuti anthuwa agwiritsa ntchito ndalamazi moyenera.

“Takhutira ndi momwe ntchitoyi yayendera. Posachedwapa, ma voluntiya athu akhala akuyendera mabanjawa kuti awone momwe agwiritsire ntchito ndalamazi,” a Maganga anatero.

Mmodzi mwa anthu omwe alandira nawo ndalamazi, a Alex Nkhoma, athokoza bungwe la Red Cross kaamba ka thandizoli, ponena kuti tsopano apeza pogwira.

Ndondomekoyi yagwiridwa ndi ndalama zokwanira K550 million m’ma boma a Mulanje, Chikwawa ndi Phalombe.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

SOCIAL COMMENTATOR SPEAKS OUT ON EXTENDED SCHOOL CLOSURE

MBC Online

Chakwera lands in Blantyre

MBC Online

World Vision vows to keep girls in school

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.