Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

‘Apatseni chisamaliro chabwino ana’

Ofesi yoona za chisamaliro cha anthu munzinda wa Lilongwe yati dziko la Malawi likhoza kudzakhala ndi m’badwo wa anthu amene sadzidzakwanitsa kupereka chisamaliro choyenera kwa ana awo mu zaka 20 zikubwerazo.

Mkulu wa ofesiyi, a Derrick Mwenda, ati izi zikhoza kukhala chomwechi ngati ana amene akukula pano sakulandira chisamaliro chokwanira chochokera kwa makolo onse.

A Mwenda amalankhula izi mu mnzindawu pa zokambirana zimene bungwe la SOS Children’s Villages linakonza zolimbikitsa kuti ana adzikula m’mabanja oyenera mmene muli makolo onse.

Iwo anapempha mabungwe osiyanasiyana kuti athandize boma kulimbikitsa mabanja kuti adzikhala odzidalira paokha ndi kumasamalira ana awo.

 

Related posts

Illegal mining threatens Zomba’s resources

Rabson Kondowe

Govt wants safe and potable water for all

Rabson Kondowe

Kusayendetsa bwino chuma ku Netball kuopseza othandiza — NAM

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.